19.02.2014 Views

KULIMA MU NJIRA YA MULUNGU - Farming God's Way

KULIMA MU NJIRA YA MULUNGU - Farming God's Way

KULIMA MU NJIRA YA MULUNGU - Farming God's Way

SHOW MORE
SHOW LESS

Create successful ePaper yourself

Turn your PDF publications into a flip-book with our unique Google optimized e-Paper software.

3) Madzi amalowa munthaka mosavuta<br />

Kulima kotembenuza nthaka: Mphamvu ya madontho a mvula<br />

imene imabwera monga nyundo pa dothi imagogomeza dothi<br />

ndikupanga chikhakha chimene chimapangitsa kuti maperesenti<br />

10 okha a mvula alowe pansi.<br />

Kulima mu Njira ya Mulungu: bulangeti la Mulungu limateteza<br />

madontho a mvula amene amabwera ngati nyundo ndipo<br />

limamwa madzi ochuluka, izi zimapangitsa kuti maperesenti 94 a<br />

mvula alowe mu nthaka.<br />

4) Kuuluka kwa madzi munthaka kumachepa<br />

Kulima kotembenuza nthaka: Ka 10 peresenti ka mvula kamene<br />

kamalowa munthaka kamapezeka kuti kakumana ndi kutentha<br />

kwambiri kumene kumapangitsa kuti madzi auluke munthaka.<br />

Kulima mu Njira ya Mulungu: bulangeti la Mulungu limapangitsa<br />

m‟thunzi pamwamba pa dothi, zimene zimapangitsa kuti pakhale<br />

chinyezi komanso pakhale pozizira, izi zimachepetsa kuuluka kwa<br />

madzi munthaka.<br />

5) Dothi lozizila zimapangitsa mbeu kukula bwino<br />

Mbeu zimene zabyalidwa pa munda wa Kulima mu Njira ya<br />

Mulungu zimatenga nthawi yaitali zisanamere, koma pakangotha<br />

masabata atatu zikamera, mbeu izi zimathamanga ndikupitirira<br />

izo zimene zabyalidwa m‟munda wotembenuza nthaka. Pamene<br />

nthaka yanu iri yozizira, zimathandiza kuti mizu yanu ikhazikike,<br />

apa mbeu yanu imakhala ya mphamvu komanso yathanzi.<br />

6) Simutaya mvula yoyambirira<br />

Kulima kotembenuza nthaka: Amadikira mvula yoyamba kenako<br />

azikalima ndi mathalakitala. Kenako amadikira mvula yabwino<br />

yachiwiri kuti abyale.<br />

Kulima mu Njira ya Mulungu: Minda imakhala yakonzedwa mvula<br />

yoyamba isanagwe. Angathe kubyala pamene mvula yoyamba<br />

yagwa pakuti madzi ochuluka samauluka ndikupita kumwamba.<br />

7) Kapalepale amakhala osavuta<br />

Kulima kotembenuza nthaka: Pamene mwatembenuza dothi<br />

zimalimbikitsa kuti udzu umere kwambiri.<br />

Kulima mu Njira ya Mulungu: Chifukwa dothi silitembenuzidwa<br />

komanso chifukwa cha bulangeti, zimathandiza kuti udzu<br />

usamere ochuluka. Kuika bulangeti pamwamba kwapezeka kuti<br />

ndi njira yabwino yogonjetsera udzu okwawa.<br />

23

Hooray! Your file is uploaded and ready to be published.

Saved successfully!

Ooh no, something went wrong!