KULIMA MU NJIRA YA MULUNGU - Farming God's Way
KULIMA MU NJIRA YA MULUNGU - Farming God's Way
KULIMA MU NJIRA YA MULUNGU - Farming God's Way
Create successful ePaper yourself
Turn your PDF publications into a flip-book with our unique Google optimized e-Paper software.
Zonse mwachidule<br />
Kulima Mu Njira Ya Mulung<br />
Kuwapatsa zida anthu osauka kuti akhale ndi moyo<br />
wochuluka mwa Khristu Yesu<br />
Dziko la Afrika liri ndi chuma chobisika chochuluka kuposa maiko<br />
onse a dziko lapansi. Liri ndi miyala ya mtengo wapatali yochuluka,<br />
zitsulo zodula komanso zitsime zamafuta, liri ndikuthekera kwakukulu<br />
pa nkhani ya zamalimidwe, anthu odabwitsa, madzi ochuluka<br />
komanso mitsinje yambiri ndi nyama zakuthengo zambiri zimene<br />
zingalipangitse dzikoli kukhala malo okuti alendo a maiko ena<br />
akanatha kumabwera ndikudzaona zinthu zimenezi.<br />
Koma mosutsana ndi kuthekera kumeneku, Afrika ndi dziko la<br />
umphwawi kwambiri, komanso anthu amakhala movutika kwambiri,<br />
kuli njala, kusowa zakudya kochuluka m‟matupi a anthu, imfa za ana<br />
zambiri, matenda, nkhondo, kudalira anthu ena, maphunziro<br />
achabechabe, kutha kwa nkhalango, katangale ndi ziphuphu<br />
komanso kusayenda bwino kwa chuma ndi kugwa kwa ndalama<br />
ngati zizindikiro zimene dzikoli likudziwika nazo.<br />
Alimi ang‟ono ang‟ono alipo okwanira maperesenti 85 mwa anthu<br />
onse a ku Afrika, amene akukhala mumoyo osowa zakudya komanso<br />
opanda chiyembekezo. Zokolola za alimi amenewa palipano<br />
ndizochepa kwambiri kotero kuti sizikutha kukwanira mabanja ao<br />
zimene zapangitsa kuti chakudya chankhaninkhani chiziitanitsidwa<br />
kuchokera maiko a kunja chaka ndi chaka.<br />
Kulima mu Njira ya Mulungu ndi yankho lodabwitsa la Mulungu ku<br />
mavuto akusowa zakudya komanso umphawi umene wagwira anthu<br />
osauka a kumudzi. Kulima mu Njira ya Mulungu siupangiri okha ai<br />
koma muli zinthu zabwino za mu Baibulo zokhuzana ndi kuyang‟anira<br />
komanso ukaswiri pa nkhani za malimidwe, kuwapatsa zida osauka<br />
kuti akathe kutuluka mu umphwawi ndi zimene Mulungu waika<br />
m‟manja mwawo komanso kuvumbulutsa chidzalo cha malonjezo<br />
ake a moyo wochuluka.<br />
1