KULIMA MU NJIRA YA MULUNGU - Farming God's Way
KULIMA MU NJIRA YA MULUNGU - Farming God's Way
KULIMA MU NJIRA YA MULUNGU - Farming God's Way
Create successful ePaper yourself
Turn your PDF publications into a flip-book with our unique Google optimized e-Paper software.
Kulima mu Njira ya Mulungu ndi mphatso yaulere ku thupi la Khristu<br />
ndipo sikwampingo ulionse ai, si kwa bungwe lina lirironse, koma ndi<br />
kwa anthu ogwira ntchito pamodzi amene anamva mumtima<br />
mwawo kuti athandize anthu osauka. Ungwiro, mayendetsedwe ndi<br />
ndondomeko za Kulima mu Njira ya Mulungu kumapangidwa ndi<br />
gulu la akuluakulu ogwira ntchito modzipereka amenenso ali akaswiri<br />
pophunzitsa.<br />
Mfundo ya kuyang‟anira osati ya umwini yakhala ikugwiritsidwa<br />
ntchito ndicholinga chokuti pakhale kufalikira kopanda malire kwa<br />
chida chimenechi chimene chingathe kusintha miyoyo ya osauka.<br />
Mau a Mulungu amati „anthu anga akuonongeka chifukwa<br />
chakusadziwa.‟ Tikuyenera kuzindikira kufunika kowaphunzitsa anthu<br />
osauka kukhala okhulupirika pa ulimi pamene kuthekera kwina<br />
kumene kuli m‟dziko la Afrika kusanavumbulutsidwe.<br />
3